Pa Mphambano Poem by Chikondi Daniel Dziko

Pa Mphambano

Liwu Lanu ndalimva
Koma ngat Yona
Mtimawu uli ndi mantha
Kodi amva?
Ndithawire kuti?

Kulira Kwa anawa nakumva
Ndi maso anga nawawona
Akufunitsitsa kuthawa Ku eguputo
Mose napemphera
Tioloka bwanji nyanjayi?

Angamve zawamisala
Ngakhale ataona nkhondo?
Ngat kotheka njirayi indipitire
Loreni nditenge inayi

Mtimawu wazizwa, pa mphambano njo!
Ndilowere kuti?
Thukuta kamu kamu napemphera
Ngat nkotheka chikhochi chindidutse
Komabe funa Kwanu kuchitidwe

COMMENTS OF THE POEM
READ THIS POEM IN OTHER LANGUAGES
Close
Error Success