Mtima Poem by Chikondi Daniel Dziko

Mtima

Mtimawu wadzadza ndi chikondi
Ngati napolo ufuna kuphulika
Tanditsepure patsayapa
Ndimpsopsono wako wadzetsa tsembwe
Udekhetse mtimawu, ulinda iwe

Ngati kanjere ka mpiru,
Ndilore ndifese chikondichi mumtima mwako
Nuchitengulira ngati mbande
Chikule monga m'bawa
Zidzulu tubvi pamthuzi pake nasewera
Iwe ndine tsitsi litabwira ufa
Pambalipo nawonera

Mtimawu ndi ng'anjo yamoto
Malawi ofukira ndi chikondi
Ndimpsopsono wako wodzetsa tsembwe
Udekhetse mtimawu, ulinda iwe

COMMENTS OF THE POEM
READ THIS POEM IN OTHER LANGUAGES
Close
Error Success