Kaomba Kamphepo ka kwathu
Dzuwa likuwala
Ana akusewera masanje
Wina nakhala mayi wina bambo
A fisi nalira dzuwa lalowa
Awa anali masewero a moyo
Kamphepo ka kwathu
Kodza kamvula katawaza
Fumbi litazilala, kadza mwa zii!
Dongo lathu titakowa
Naumba galimoto
Ena naumba za mawaya ena za njerwa
Awa anali maloto athu
Nyau! Nyau!
Kadza ndi mfuwu kamphepo kakwathu
Zonse Nataya liwiro Kobo!
chipako nda amakaka
Akapoli nda kamano tithamangitsana
Wasilamba patsogolo chilembwe napita
Awa anali magule akwathu
This poem has not been translated into any other language yet.
I would like to translate this poem